Phwando la Mkate Wopanda Chotupitsa limaphatikizana ndi mzimu wa nsembe, kudzipereka, ndi chikondi cha Khristu amene anadzipereka Yekha kuti apulumutse anthu amene anachimwa kumwamba. Tiyenera kukumbukira Phwando la Mkate Wopanda Chotupitsa, ndi cholinga cholapa machimo athu kudzera pa kupachikidwa ndi moyo wa Khristu, ndi kutenga nawo mbali mosangalala m’masautso Ake.
Mulungu anadza padziko lapansi chifukwa cha chipulumutso cha anthu, komabe ngakhale Petro, wodziwika chifukwa cha chikhulupiriro chake, Yudasi Isikariote, ndi ophunzira ena onse anachita zinthu zoopsa pamaso pa Mulungu. Kuphunzira chikondi cha Mulungu, amene sananyoze ochimwa oterowo koma anawachitira chifundo, tsopano tiyenera kuyenda m’njira ya chikhulupiriro chokhala ndi mtanda wathu.
Koma izi zonse zinachitidwa,
kuti zolembedwa za aneneri
zikwaniridwe. Pomwepo
ophunzira onse anamsiya
Iye, nathawa.
Mateyu 26: 56
Pomwepo Yesu anati kwa ophunzira
ake, Ngati munthu afuna kudza
pambuyo panga, adzikane yekha,
natenge mtanda wake, nanditsate Ine.
Mateyu 16:24
119 Bundang P.O.Box, Bundang-gu, Seongnam-si, Gyeonggi-do, Rep. of KOREA
Tel 031-738-5999 Fax 031-738-5998
Likulu la Ofesi: 50, Sunae-ro, Bundang-gu, Seongnam-si, Gyeonggi-do, Dziko la Korea
Mpingo Waukulu: 35, Pangyoyeok-ro, Bundang-gu, Seongnam-si, Gyeonggi-do, Dziko la Korea
ⓒ Gulu la Utumiki wa Dziko Lonse la Mpingo wa Mulungu. Ma Umwini onse ndi Otetezedwa Mfundo za Zinsinsi